15.The Rock

  1. Alif Lam Ra. Awa ndi mavesi a Buku, ndipo ndi Korani yofotokoza bwino
  2. Mwina iwo amene sakhulupirira adzafuna kuti akadakhala Asilamu
  3. Alekeni kuti adye, ndi kuti asangalale ndipo alekeni kuti atangwanike ndi chikhulupiriro chabodza. Iwo adzadziwa posachedwapa
  4. Ndipo Ife sitinaonongepo mzinda wina uliwonse, kupatula pamene nthawi yake itakwana
  5. Anthu sangathe kufulumizitsa chionongeko chawo kapena kuchichedwetsa ayi
  6. Iwo amati, “Iwe, amene Korani yavumbulutsidwa kwa iwe! Ndithudi ndiwe munthu wa misala.”
  7. “Bwanji siutibweretsera angelo ngati iweyo uli mmodzi mwa onena zoona?”
  8. Ife sitimatsitsa pansi angelo, kupatula ndi choonadi ndipo zitatero iwo sadzapatsidwa nthawi
  9. Ndithudi ndife amene tidatsitsa Korani ndipo, ndithudi, Ife ndife amene tidzaiteteza
  10. Ndithudi Ife tidatumizapo, iwe usanadze, Atumwi ena pakati pa mibadwo yakale
  11. Ndipo sikunadze kwa iwo Mtumwi, amene iwo sanamuchite chipongwe
  12. Kotero timalowetsa chisokonezo m’mitima ya anthu ochita zoipa
  13. Iwo sangakhulupirire mu uthenga wa Korani ndipo ndi chizolowezi cha anthu amene adalipo kale
  14. Ndipo ngati Ife tikadatsekula khomo lakumwamba, iwo ndi kumakwera kumwamba mosalekeza
  15. Iwo akadakanabe kuti, “Maso athu athobwa. Ndithudi ife talodzedwa.”
  16. Ndithudi Ife taika nyenyezi zikuluzikulu kumwamba ndipo tazikongoletsa kuti zizikondweretsa anthu oyang’ana
  17. Ndipo tawateteza malo a kumwamba kwa Satana wotembereredwa
  18. Kupatula iye amene amamvetsera mwakuba, iye amatsatiridwa ndi malawi a moto
  19. Ife tidatambasula dziko lapansi ndi kuikamo mapiri ndipo tameletsa mu ilo zinthu zosiyanasiyana chilichonse chili ndi muyeso wake
  20. Ndipo takupatsani mu ilo njira zopezela chakudya chanu ndi cha izo zimene inu simungathe kuzidyetsa
  21. Palibe chilichonse, chimene nkhokwe yake siili ndi Ife ndipo sititumiza kupatula m’muyeso wodziwika
  22. Ndipo Ife timatumiza mphepo yobereketsa ndipo timatsitsa madzi kuchokera kumwamba ndipo timakupatsani kuti mumwe; ndipo inu si ndinu osunga nkhokwe zake
  23. Ndipo, ndithudi, Ife ndife amene timapereka moyo ndi imfa ndipo zinthu zonse ndi zathu
  24. Ndipo, ndithudi, Ife timadziwa onse amene adalipo kale inu musanadze ndipo timadziwa mibadwo yanu yatsopano ndi iwo amene adzadza m’tsogolo
  25. Ndipo, ndithudi, Ambuye wako adzasonkhanitsa onse pamodzi. Zoonadi Iye ndi Wanzeru ndi Wodziwa chilichonse
  26. Ndipo, ndithudi, Ife tidamulenga munthu kuchokera ku dothi lotulutsa mawu, losinthidwa m’matope akuda osalala
  27. Tidapanga mtundu wa majini poyamba kuchokera ku mphepo ya moto
  28. Ndipo pamene Ambuye wako adati kwa angelo, “Ine ndilenga munthu kuchokera ku dothi lotulutsa mawu losinthidwa matope akuda osalala.”
  29. “Motero ndikatha kumukonza ndi kuuzira mpweya umene ndidalenga chifukwa cha iye ndipo nonse gwadani kumulambira iye.”
  30. Motero Angelo onse adagwada ndi kumulambira
  31. Kupatula Satanaadakanakukhalammodzimwaolambira
  32. Mulungu adati, “oh iwe Satana! Kodi ndi chifukwa chiyani siuli pamodzi ndi olambira?”
  33. Satana adati, “Ine sindingagwadire munthu amene Inu mwamulenga kuchokera ku dothi lotulutsa mawu losinthidwa matope akuda osalala.”
  34. Mulungu adati: “Motero choka kuno chifukwa ndithudi iwe ndiwe wotembereredwa.”
  35. Ndipo, ndithudi, temberero lidzakhala pa iwe mpaka pa tsiku lachiweruzo.”
  36. Satana adati, “oh Ambuye wanga! Bandisungani mpaka patsiku louka kwa akufa.”
  37. Mulungu adati, “Ndithudi iwe uli m’gulu la anthu amene apatsidwa nthawi.”
  38. “Mpaka pa nthawi ya tsiku lotsimikizika.”
  39. Satana adati, “Oh Ambuye wanga! Popeza Inuyo mwandisocheretsa ine, ndithudi, ndidzawasalalitsira njira yautchimo anthu onse padziko lapansi, ndithudi onse ndidzawasocheretsa
  40. Kupatula akapolo anu osankhidwa amene ali pakati pawo.”
  41. Mulungu adati, “Imeneyi ndiyo njira imene idzalondola mwachindunji kwa Ine.”
  42. “Ndithudi iwe siudzakhala ndi mphamvu pa akapolo anga, kupatula anthu ochita zoipa amene amakutsatira iweyo.”
  43. “Ndipo, ndithudi, Gahena ndi malo olonjezedwa kwa iwo onse.”
  44. “Iyo ili ndi makomo asanu ndi awiri, ndipo chipata chilichonse chidzakhala ndi anthu ake olowapo.”
  45. “Ndithudi! Onse oopa Mulungu adzakhala m’kati mwa minda ndi m’kati mwa a kasupe.”
  46. “Lowanimo mwamtendere mopanda mavuto.”
  47. “Ndipo Ife tidzachotsa m’mitima yawo mkwiyo uliwonse kuti akhoza kukhala pachibale ndi kupumula m’mipando yawofowofo moyang’anizana.”
  48. “Ndipo iwo sadzatopa kumeneko ndipo sadzafunsidwa kuti achoke ku Paradiso.”
  49. Auze akapolo anga kuti ndithudi Ine ndimakhululukira ndipo ndine wachisoni
  50. Ndiponso kuti chilango changa, ndithudi, ndi chilango chowawa koposa
  51. Auze za alendo a Abrahamu
  52. Pamene iwo adadza kwa iye ndi kumuuza kuti, “Mtendere ukhale kwa iwe.’ Koma iye adawayankha kuti, “Ndili ndi mantha ndi inu.”
  53. Iwo adati, “Usaope! Ife tadza kwa iwe ndi nkhani yabwino ya mwana wamwamuna amene adzakhala wodziwa zambiri.”
  54. Iye adati, “Kodi inu muli kudzandiuza nkhani yabwino pamene ine nditakalamba kale? “Kodi nkhani yanu ndi yotani?”
  55. Iwo adati, “Ife tili kukuuza nkhani yabwinoyi mwachoonadi. Kotero usakhale wotaya mtima.”
  56. Iye adati, “Ndani amene angataye mtima ndi chifundo cha Mulungu, kupatula osochera?”
  57. Iye adatinso, “Kodi cholinga chanu ndi chiyani, inu otumidwa?”
  58. Iwo adati, “Ife tatumidwa kwa anthu oipa.”
  59. “onse kupatula anthu otsatira Loti okha. Ife, ndithudi, tidzawapulumutsa iwo okha.”
  60. “Kupatula mkazi wake amene ife talamulidwa kuti akhalire m’mbuyo pamodzi ndi iwo amene anali kukhalira m’mbuyo.”
  61. Ndipo pamene a Kazembe athu adadza ku nyumba ya Loti
  62. Loti adati, “Ndithudi inu ndinu anthu omwe sindikudziwani.”
  63. Iwo adati, “Iyayi. Ife takubweretsera iweyo zinthu zimene iwo anali kukayika.”
  64. “Ndipo Ife tadza ndi choonadi kwa iwe ndipo, ndithudi, ife ndife onena zoona.”
  65. “Motero choka ndi abale ako pakati pa usiku, iwe uziyenda pambuyo pawo ndipo usalole wina aliyense kuti atembenuke. Kapita kumene walamulidwa kupita.”
  66. Ndipo tidamuuza lamulo ili kuti mizu ya iwo idzazulidwa m’mawa
  67. Ndipo anthu a mu Mzinda adadza ali osangala
  68. Iye adati, “Ndithudi! Awa ndi alendo anga motero musandichititse manyazi ayi.”
  69. “opani Mulungu ndipo musandipangitse manyazi.”
  70. Iwo adati, “Kodi ife sitidakuletse kuti uzichereza alendo?”
  71. Iye adati, “Awa ndi ana anga a aakazi; akwatireni ngati inu mufunadi kutero.”
  72. Ndithudi pali moyo wako! Iwo chifukwa chakuledzera anali kuyenda mwakhungu
  73. Ndipo chilango chidawapeza pamene dzuwa linkatuluka
  74. Ndipo Ife tidaononga (mizinda yawo) zapansi kukhala pamwamba ndipo tidawagwetsera mvula ya miyala ya moto
  75. Ndithudi! Mu izi muli zizindikiro kwa anthu omvetsa
  76. Ndipo, ndithudi, iyo ili m’mphepete mwa msewu umene umapitidwa
  77. Ndithudi! Muizimulizizindikirokwaanthuokhulupirira
  78. Ngakhale anthu okhala m’nkhalango nawonso anali ochimwa
  79. Motero Ife tidawalanga. Ndipo iwo ali pamalo poonekera
  80. Ndipo, ndithudi, anthu a ku Hijr adakana Atumwi
  81. Ndipo Ife tidawapatsa zizindikiro zathu koma iwo adazikana
  82. Ndipo iwo anali kukumba mapiri kukhala nyumba zawo ndipo anali kukhala mosaopa
  83. Phokoso la chilango lidafika kwa iwo m’mawa
  84. Ndipo sizidawathandize zonse zimene anali kuchita
  85. Ndipo Ife sitidalenge kumwamba ndi dziko lapansi ndi zonse zimene zili pakati pawo kupatula ndi choonadi. Ndithudi popanda chikayiko tsiku lachiweruzo lidzadza; kotero akhululukireni, kukhululuka kwabwino
  86. Ndithudi Ambuye wako ndi Namalenga ndi wodziwa zinthu zonse
  87. Ndipo, ndithudi, Ife tidakupatsa mavesi asanu ndi awiri amene amanenedwa kawirikawiri ndi Korani yolemekezeka
  88. Usamayang’ane mwanjiru zinthu zokoma zimene tawapatsa ena a iwo kapena kumamva chisoni pa izo. Ndipo onetsani chifundo kwa anthu okhulupirira
  89. Ndipo Nena, “Ine ndine Mchenjezi”
  90. Monga tidatumiza kwa amene amagawanitsa
  91. Amene apanga Buku la Korani kukhala magawo awiri
  92. Kotero, pali Ambuye wako, tidzawafunsa
  93. Pa zonse zimene anali kuchita
  94. Motero lalikira poyera zonse zimene walamulidwa, ndipo choka pakati pa osakhulupirira
  95. Ndithudi Ife tidzakuteteza kwa onyoza
  96. Iwo amene amatumikira mulungu wina kuonjezera pa Mulungu weniweni iwowo adzadziwa
  97. Ndithudi Ife tilikudziwakutizimakupweteka mumtima mwako zinthu zimene amanena
  98. Motero lemekeza Ambuye wako ndipo khala mmodzi wa iwo amene amagwada pomulemekeza Iye
  99. Ndipo pembedza Ambuye wako mpaka pamene ola lotsimikizidwa likupeza